Zodabwitsa zongochitika kumene

Zodabwitsa zongochitika kumene Zikachitika mumvera kwa ife

13/03/2026



Bambo wina yemwe sakudziwika wapezeka atafa komanso thupi lake litawonongeka mu mtsinje wa Bua m'boma la Ntchisi.

Wachiwiri wa wofalitsa nkhani za apolisi m'bomali, a Tadala Makiyi, wati thupi la bamboyu lapezeka likuyandama mu mtsinjewu lachinayi sabata ino.

"A Manuel Mwenje, a mmudzi wa Matekenya mfumu yaying'ono Kabvulala, anathamangira ku polisi ya Malomo ataona thupili," atero a Makiyi.

Iwo ati zotsatira zachipatala, zatsimikiza kuti bamboyu anamwalira kaamba kobanika chifukwa chomira.

Pakadali pano apolisi m'bomali, akusakasaka achibale a malemuwa.

Wolemba: Abdul Kalonga

  Pambuyo pa mphekesera zomwe zakhala zikuveka, zatsimikizika tsopano kuti Brian Banda wasankhidwa kukhala mkulu wa wail...
13/03/2026




Pambuyo pa mphekesera zomwe zakhala zikuveka, zatsimikizika tsopano kuti Brian Banda wasankhidwa kukhala mkulu wa wailesi ya boma ya Malawi Broadcasting Station (MBC).

Malingana ndi kalata yomwe wasainira wapampando wa bodi ya wailesiyi, Dr Benson Tembo, Banda akuyembekezeka kuyamba ntchito Lolemba, pa 16 March 2026.

Bodiyi yati ikukhulupirira kuti kusankhidwa kwa Banda ndi gawo lofunika kwambiri lolimbikitsa utsogoleri wa wailesiyi komanso kupititsa patsogolo udindo wa MBC wopereka mauthenga odalirika, aukadaulo kwa a Malawi, ndipo yapereka mafuno abwino kwa Banda.

Asanasankhidwe paudindowu, Banda amagwira ntchito ku Times Group. Iye akulowa mmalo mwa Moses Chiwoni yemwe adasankhidwa ngati woyembekezera chabe kutsatira kuyimitsidwa komaso kuchotsedwa pa ntchito kwa George Kasakula.

Wolemba Archangel Nzangaya

07/02/2026

Mwai wantchito maid akufunika Zomba winaso Blantyre
Contact admin no qualifications required

16/01/2026

Mwai wantchito pa filling station limbe MSCE basi
If ur serious contact admin

Happy holidaysChilembwe day our freedom fighter
15/01/2026

Happy holidays
Chilembwe day our freedom fighter

Caroline Alick yemwe wakhala akupempha thandizo la makina oti azimuthandizila kupuma, wamwalira 😭💔Msungwanayu anali ndi ...
14/01/2026

Caroline Alick yemwe wakhala akupempha thandizo la makina oti azimuthandizila kupuma, wamwalira 😭💔

Msungwanayu anali ndi matenda a m'mapapo (interstitial lung disease) omwe madotolo anamupeza nawo m'chaka cha 2025.

Malinga ndi mayi a msungwanayi, a Aisha Alick, Caroline wamwalira manasana a Lachitatu akulandira thandizo la chipatala cha Mua Mission.

Caroline anali ndi zaka 19, ndipo amachokera m'mudzi mwa Mwaiwaza 2 mfumu yayikulu Kachindamoto m'boma la Dedza rest in peace baby girl walimbana nako kulimbana kwabwino 😭😭
RIP

Mpulumutsi wathu wathu long live atate
14/01/2026

Mpulumutsi wathu wathu long live atate

14/01/2026

Pano izitchedwa FDH Premiership owina azitenga 200 million

TNM Superleague yatha bas

13/03/2025

Kwagwanji kumene muli inuko call us now 0992672233
Cyclone Jude waononga motan kwanuko

18/12/2024

More news coming soon stay tuned

19/07/2024

17 k page for sale guys admin is selling this page

Address

Chitawira
Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Zodabwitsa zongochitika kumene posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Establishment

Send a message to Zodabwitsa zongochitika kumene:

Share