BEST HES's stories

BEST HES's stories Writer, Musician & Up coming Actor

https://youtube.com/?si=Gtba2CH1FtWHae0N

14/06/2025

SECOND PART OF BROKEN PARTY 🔇🔇🔇🔇🔇
Story written by HENRY MKWAILA...🖊️

CONT.
Hassan: Chabwino ndanva Maganizo ako nane ndimasaka True Love
Lita: Wow Ngati kutulo, sindikukhulupilira kuti ndakuwinadi ....... ..
Moyo wamuchikondi unayambika zonse zimayenda bwino aliyense nde amakhutira kuti akupatsidwa True Love ija moti Sitimalora kusowana kwakanthawi, nthawi zonse ma foni amakhala ali mmanja Kuyankhulana ngati tikuonana maso ndi maso kotero zoti tili motalikanabe sizimaoneka ......
....
Tsiku lina ndili khale ndinalandira Foni kuchokera kuja ndinakapanga Interview kuja yondiitana kuti ndikayambe ntchito ndipo ndinasangalala mnajowajowa anga kamwana kang'ombe, mosachedwa ndinamuuzanso Lita ndipo naye anazikonda....

Kuchokera nthawi yomwe ndinayamba ntchito zinthu zina ndi zina pakati pa ine ndi Lita zinayamba kusintha monga kuyambana yambana kunayambika ndipo kumachitika pafupi pafupi chifukwa samandinvetsetsabe kuti andipatse mpata ogwira ntchito chifukwa ndikachedwa Kuyankha foni yake amazinva ngati ndasiya kumukonda, kwa ineyo ndimazinvetsetsa komano ndinazivomereza kuti ndizikhala Kaye ngati ndaipa koma mwina akazindikira andinvetsetsanso naye komanso azolowera komabe ai ndithu pena zimazakhala ngati wayamba kundinvetsetsa koma pena umazakhalanso Moto komabe Chikondi Chathu chimapita Chitsogolo

Hassan: Wachikondi wanga ndaganiza Zoti tikhale Moyandikana mwina zitithandizira kuchepetsa mikwiyo

Lita: Zoona Wow! My Handsome ndachita kunva kukoma Pali ponse thupi langali mmh Nsane iwe ndi mdalitso mmoyo mwanga, umaziwa Kukonda ndipo wakwanitsa Kuziwa Zosowa zanga iwe ndi king wanga

Hassan: Wakondwa tu

Lita: Eya ndipo apa nde mwezi wamawa Birthday yako ndizomwe ndimakhumba ndikufuna nzapangitse Party tizasangalalire kubadwa Kwako ndipo usadere nkhawa chili chonse ndizapanga ine

Hassan: umapangiranji zonsezi zomwe ndimayenera ineyo ndizikupangira iweyo ?

Lita: ine ndinakonda mtima wako basi
......
Tinakambirana zambiri pamenepaja chinatsalira ndikumangodikira masiku kuti tikafike ku tsiku Lolonjezedwalo ndipo kwaineyo ndimati ndikalingalira ndimaona kukhala tsiku lokoma komanso lapamwamba izi zinandipangitsa Kuona Kuchedwa .....
Tili mkati modikilira ...
Weekend ina ndinaganiza zopita kumudzi kukawona makolo ndipo nditafika kumene kuja ndinacheza bwino bwino kufikira nthawi yomwe ndinafuna kubwelera komwe ndimakhala koma ndisananyamuke amai anandiimitsa mooneka kuti pali chomwe chachitika ndipo nkhani yake ndiyaikulu ndipo zokhazo zinali zokwanira kuti mtima wanga uthamangitse Mwanzi kupopa mwankhanza muja .......

Mai: Kodi nthawi ina yake unangoti ukufuna ukwatire wapeza mkazi ndizoti unali serious kapena zanthabwala

Hassan: mmh Amai nkhani ngati imene ija ndikakambe zanthabwala? Komano chachitika ndichani ?

Nditawafunsa anangondionetsa nambala ya foni kenako mkuzandifunsa kuti ndikuiziwa nambala imeneyo ndipo ndinawauza kuti Eya .....

Mai: Munthu ameneyu anaimba nde anafotokoza zoti ndi mkazi wako nde ndichifukwa ndakumbukirano kuti unayankhulapo zoti wapeza mkazi komano tisanapite patali kodi Mkazi ali ndi mwana wako uja zili pati pano

Hassan: Choyamba ndiuzeni kaye mwamuyankhula kuti chani Lita??

Mai: ndakufunsa nde ungondiyankha

Hassan: Amaiiii !!!! Oh Komano mukuziwa kale mene zinakhalira ndinamuiwala kale kale pano munthu anandiuza ekha ndikamwa yake Kuti amupezera mamuna ndipo ndisamaimbe ndimusokonezera banja mpaka pofika kundi block nde ine ndikanatani basi nane mnamuiwala apa ndapeza nzanga amene ndikunvetsetsa naye

Mai: zinatero mwina ndi eya komanso ndi Ai mwina amangoyankhulira Kupsa mtima komano zinakhalabe bwino chidzukuli changa cho chidzidzakwanitsa kuwayendera agogo akene zamaudanizi sizindisangalatsa ine

Hassan: Amai mwini chisankho ndine ndisiyeni, kodi simungasangalare mutamandiona ndili wachimwemwe ?? Mmansangalala ndikamakhala muzinkhawa ?? Tayeseraniko kusamalanso zachimwemwe ndi mwana wanune, kukazakhala kwa Mwai chidzukulu chanucho nzakachitenga muzizamuona mene mungafunire Komanso ndi Lita tizakupangirani Chizukulu

Mai: Uziyankhula mondipatsa ulemu ndine mayako

Hassan: Eya koma nanu mukuyenera kusamala zachimwemwe cha Mwana wanu Lita ndimamukonda ndipo amandikonda

Mai: nde ukupita tisanamalize kuyankhulana ? Paja nawe suchedwa Kupsa mtima koma ukanabwelera tizilongosore zimenezi .....
.......
Ndinakanika kuwayankhanso pamene paja mpaka ndinanyamuka titakwiitsana, ndinali Obalalika ndi Okwiya mutsiku li, ndipo nditangofikanso kunyumba Lita kumaimba Foni .....
Lita: tsiku lonse osandiyankhula? Komano mwangoyenera Pepa sindimaziwa kuti uli ndi Banja

Hassan: zimenezo nso nde ziti ?

Lita: Mmh Zitaye komano lero ndinayankhula ndi amai andiuza kuti uli ndi Mkazi komanso mwana

Hassan: Mau anga ndiopanda Ntchito kwa iwee kodi ?? ndizomwe umaimbira foni kuti uzindifufuza ?? Chabwino ulibe nthawi yondifunsa koma kundifufuza nde pitiriza zomwezo Osandibhowa nso apa

Lita: iiiiih Hassan ndimakukonda sinati ukwiye apa ine

Hassan: Bola wadziwa kuti ndili ndi mkazi nde mwina nthawi inakuchepera zifufuza kaye kuti ndine Otani ndikupatsa 35 Days I think panopa tipatsane kaye nthawi kuti aliyense amuziwe nzake kenako tizizawona chitsogolo kuti Chikondi chathu ndichotheka kapena ai

Lita: Eya ndiza bho bho basi tiyeni tidikire masiku wo ......
....
Chikondi chinafika Popempha Break ,,,
Moyo unali owawa pokhala mozisowa zomwe ndinazolowera kufikira pomwe ndinakanika kupilira mpaka ndinamuhalla Lita kuti ndiziwe za Moyo wake

Hassan: apa tili pa half ya 35 Days ija Nde tandiuze moyo wako ukuyenda bwanji ?

Lita: nthawi zonse umayenda bwino

Hassan: Ooh owo ndekuti zili bwino Chabwino ndimafuna ndiziwe kuti munthawi imeneyi ngati ufunikire njira zina zopezera ma information okonzera ubale wathu ....

Lita: sindikufunikiranso kali konse ndipo ndikafuna kachani ngati pakati pathu pali ubale uli onse ?

Hassan: Ukutanthauza chani

Lita: kodi mesa unathetsa Chibwezi nde sizofunikira zimenezo zipangani zoti zizikuthandizani mukafuna ine tingathe kungokhala ma friend chabe kucheza ndiza bho bho

Hassan: Aaah iweee ashiiiii bwanji ukupitiriza kuononga zinthu ? Ndimaganiza kuti kwanthawi ndinapereka ija zitithandiza kudekhetsa mitama yathu ndipo aliyense akwanitsa kuzifufunza vuto lake ndikulikonza koma ayi ndipamene zikuonongekerabe nditani kuti zikonzeke

Lita: Aaah usapange kali konse zisiye Choncho tiyeni tizingocheza basi ngati wina ndi nzake

Hassan: Oh zikomo Pachimenecho koma sizofunikira nde zitaye Basi amoyo salekana tizaona ukhale ndi nthawi yako yopambana
......
Ndinayankhula ngati zukoma koma mumtima misozi ikutsika, Moyo sumakoma nso. Masiku amapitadi ine ndi Lita kuli ziiii .... Masiku a Birthday yanga anayandikira ndi azizanga omwe ndinawaziwitsa za Party anayamba kundifunsa zamadongosolo ngakhale ndimawayankha zosanveka koma ndimawalimbitsa mtima kuti chili chonse chili Set ......

Tsiku litafika Sindinavute vute Tinapeza Dj wazoimba zabwino komanso kugula zakudya ndizakumwa kuti Chikondwelero chichitike Monga ndimkakhumbira Lita ali pambali panga tikusangalalira limodzi tsiku li koma ngati mmaloto ndimangoona chithunzi thunzi chake chokha, kotero zinandivutabe kukhala pamalo paja ndipo ndinachokapo kuwasiya anthu ali mkati mwa madyelero ndikumwelera uku choimba chikusinja zantchito zija .... Nthawi itafika yoti andifunire mafuno abwino anthu anali odabwa kuti sindimaonekapo ndipo mchimwene sanachedwe koma kuimba foni kufunsa zakomwe ndili .....

"" Oh sorry mchimwene koma sindikwanitsa kupanga nawo zimenezo ndipo ndatalikira basi kwaine ndizosakwanira kupezeka pamenepo""

Mau wa Mchimwene anakhumudwa nawo ndipo foni isaduke ndili mkati monvetsera anayankhula tu kwa anthu onse omwe anabwera ku party yi

"Party yi ithere p***a basi this is BROKEN PARTY 🔇"

END OF STORY

11/06/2025

BROKEN PARTY
🔇🔇🔇

Onamawo paja Amati Chibwezi Chongoyamba Kumene kukoma mmmh 😊😊😊

"Hassan..... Kubwerako mmoyo mwanga unasintha zambiri ndipo nane ndakonzeka kusintha dziko lako"........

"Lita ukunena zoona ??"

" Eya zoona nde Big Celebration izakhale pa Birthday yako bola asakhale ngati masiku adutsa kale "

" Ai ndi mwezi wa Mawa ndinabadwa pa 21 November Koma ukazapangapangadi party imeneyo mmh kazakhala koyamba kanga kukhala ndi party yosangalalira kubadwa kwanga"

" Wow, ndizatero chomwe ndikungofuna mmoyo mwanga ndichoti uzikhala osangalala Mamuna wanga nde BIRTHDAY PARTY ilipo mwezi wamawa"

" Zikomo kwambiri ndipo umandipangitsa kuti ndisamanvetsabe kuti mwaine unaona chani Lita? Mpaka kulimba mtimadi kundifunsira iweyo".....
.....
Hahaha Lita anaona chani mwa Hassan ? .....

Dzina langa ndine Hassan nde tiyambe motere, tsiku lina ndinali ndi ulendo wanga kuchokera kopanga ma Interview antchito ndipo min bus yomwe ndinakwera ndinakhala Moyandika ndika Mtsikana komwe kamachita kuwala mothobwa mmaso, ndisanene zambiri komano nkhani ndiyoti anali mkazi okongola zija zoti ndimakanika ndikungomupatsa moni emwe kuli kuopa 🤗😁

Tili mkati mwa Ulendo, mosayembekezera Duwa lija linaponya mau kwaine omwe ndinawayankha mwachibwibwi chifukwa sindimayembekezera .....

"Oh ndine Lita, mwachidule ndikutsika p***a nde tangondipatsa nambala yako ya foni chifukwa zomwe ndimafuna kunena sinanene tu apa"..........

Ndinapereka Nambala ija kenako anatsika mkumapita uku nafenso kumapitilira, zinthu zake zimachitika mondibalalitsa nsaname chotsatira ndimangodikira kuti andiuza zotani ndipo usiku watsikuli mnadikira kuti ndiimbilidwa foni koma ai kunalii zii ndipo mnadziwa kuti amangodoja ameneyo mwina inali tease chabe

Patangodutsa ka 2 days nditaweruka tsiku limenelo kuganyu kwanga ndiwu batchala wanga, ndili mkati moziphikira foni inasokosera ndipo mosachedwa mnapita kukaikhazika Chete....
Phone: Hey man ndine Lita
Ine: Oh yah ndakukumbukira
Lita: Yap nde tisanapite patali sindikudziwa kuti nthawi ndaimba yi ndiyolondola chifukwa ukuyenera kundiuza ngati uli ndi banja kuti ndiziziwa nthawi yoyenera kukuimbira kuopa kukuyambanitsa ndi Sosobina yako
Ine: hahahah Aaah waganiza bwanji, Anyway sunalakwitsedi kufunsa komano ungathe kumamuimbira nthaw ili yonse Batchala yu
Lita: Ah Ok nde ndingophika kaye ndikuimbirabe ......

Apa nde zinayamba kundinvekeranso mwa Mtundu wina ,, "Mmmh nde mwati mkazi ameneyu ndiwota, Oh ndiomasuka munthu yu" .....
Macheza atsiku li anapitira ataimbanso kachikena apa nde uchinzake unayambika koma nthawi zonse potsanzikana tikanaliza kucheza amakonda kundisiya munkhalango yamaganizo ....
Lita: Ndatopa ndigone tipitiriza mawa kucheza chifukwa apa pali nkhani yoti ndikuuze ....
Anangotero kenako kuzimitsa Foni pompo tu eti nde kaya naye samadziwa kuti mene anangoteromo asokoneza Tulo langa hhhm kaya bola iye anakwanitsa kugona koma ine nde mnachezera ndithu ....
..
Tsiku lotsatiralo macheza anayambika ndipo nkhani amandifunira ija tinaikambirana motere;,,,,,,,,,,,,
Lita: ndikufuna Ndikukwatire Hassan
Hassan: 🤗😁😁 koma ndusowa kuti ndiseke kapena ndilire Anyway ma Joke akowa dzulo andikanikitsa Kugona ine
Lita: Hassan sindiku Joke ine ndili serious nde ndiuze wandilora kapena wandikana ?
Hassan: hahaha ndakukana
Lita: ukuseka ngati zoseketsa bwanji ? Ndikuuze motani kuti sindiku joke ?
Hassan: Chabwino komano ukuziwa sindikuziwa kuti walimba mtima motani mpaka kuthira vibe munthu Oti sitikudziwana or uli iwe sungadabwitsike ?
Lita: Mwina di ndizotero koma ineyo mbali yofikira chikondi changa mwaiwe ndikuidziwa ndipo ndinakudziwa kale kale ndiponso ndinayamba kukusaka kale kale koma mwai wagwa pano kuti njira yolumikizirana yapezeka nde ndidikire nso chani kukuuza zomwe ndakhala ndikukhumba kwanthawi yaitali
Hassan: Wow !, zodabwitsa kwambiri, koma ineyo nde sindikudziwadi kali konse
Lita: Chabwino ndakwanitsa kukuuza mawuwa mwina poti unangondiuza kuti suli pabanja ndekuti ukukanika kundivomera chifukwa choti uli ndi chibwezi Chabwino ingondimasula tipeze njira ina
Hassan: Sindili pabanja eya Komanso ndilibe Chibwezi pakadali pano kufikira munthawi yake ikadzakwananso
Lita : Chabwino nde ingondilora ndikhale nzako wapamtima
Hassan: Oh yah Chinzake sicholetsedwa tingathe kutero uli olandilidwa ......
........

Macheza amapitilira mwachinzake chabe koma mwapang'ono pang'ono zinafika poti aliyense amakhumbirano nzake koma ndimakanika kumuuza Lita kuti nane ndagwa naye mchikondi chifukwa ndinali ndimafunso omwe ndimakanika kuziyankha kotero ndinangopeza nthawi yake kuti ndiziwe zambiri ......
Hassan: komano iweyo mene wakongoleramo ndizosatheka kukhala Opanda chibwezi nde bwanji ukundiyesa ine ?
Lita: ndinkhani yaitali ndipo inenso mtakufunsa ngati zomwezi unakanika kufotokoza unangoti ndinkhani yaitali komano ineyo ndili okonzeka kukuuza
Hassan: Kungoti ndimaziimba mlandu ndekha nde ndikamazikumbukira zimandinvetsa chisoni ndichifukwa ndimakanika kukuuza komano pepa Ndikuuza panopa
Lita: Chabwino koma ndiyambe ineyo ndikamaliza ndekuti nawe undiuzanso.... Lita anayambapo kufotokoza munyengo zomwe anadutsa kuti akapezeke munyengo imeneyo ndipo zina mwa izo anafotokoza motere;......
"Panthawi yomwe ndinapanga Chibwezi choyamba ndinazilonjeza kuti ndizagona ndi mamuna pokha pokha tizakwatire ndipo izi nthawi yambiri zimadzetsa mkangano muchibwezi chathu chifukwa akandifuna ine ndimamukanira mpaka anafika pothetsa Chibwezi.... Patapita nthawi ndinapanga Chibwezi china, apa ndinali nditayamba kukhwima munzeru ndipo ndinayamba kumazitolera kuti chikondi ndichani ndimene amandikondera mamuna ameneyo ndinabalalika nacho chikondi kunena zoona ndinafika pomangokhala ngati munthu opanda nzimu chifukwa sindimakwanitsa kupanga chiganizo koposa kumangomunvera bwezi langalo mpaka popereka Unamwali wanga pa iye ..... Kupita kwa nthawi ndinamupempha kuti ndikufuna foni, sanandikanire anangoti mkundipatsa yake ndipo zinatero koma ichi chinali chiyambi chakukhumudwanso kamba koti anazasiya foni kuiwala ku delete zomwe amacheza ndi akazi ena mmh Saname inali nyengo yowawitsa maka ndinazindikiranso kuti amagona nso ndi nzanga wapamtima ,,,,, Ndinathetsa chibwezi koma moyo nde unalowelera mpaka kufika pofuna kuzipha koma anali mchimwene anandipulumutsa tameki Okumwa imwa ndimwachikondi chake anandisungira chinsinsi posamuuza aliyense chabe anangondilangiza kuti simathero amoyo amenewo......
Mozilimbitsa mtima ndimakhaladi uku pang'ono ndipang'ono ululu unanveka ngati ukufuna uyambe kuchepa koma sizinatheke chifukwa mwezi utatha ndinadabwa masiku anga akwana koma sindikusamba mwamantha kupita kuchipatala anandipeza kuti ndine oyembekezeratu, Hassan tangoganiza apa ingakhale nyengo yowawitsa bwanji ?"........

Nkhani yonse tu mkuti tikukambirana pafoni ine ndi Lita yo koma anafika pena pokanika kuyankhula kuli kulira ......

" Eyetu Hassan ndekunena zoona ndili ndi Mwana Modzi (Emmanuel), iweyo ndimakuona kwambiri kunkhani za Hes pa Page yake ndipo muzambiri ndikamakuonako unafika pondipatsa chikoka kuti ndiwe mamuna odziwa chikondi kwambiri ndimangopereka ulemu kuti Mkazi wako ndiwa mwai kukhala ndi mamuna ngati iwe, ndipo ndinakonda kuti tizakhale pachinzake kufikira tsiku tinakumana lija komano pondiuza kuti ulibe mkazi wanditengera ku mulingo wina Hassan ndakhumba kukhala mkazi wamwai yo komano ndikuzinva ngati sindingapeze mwai kwaiwe chifukwa ndiwe mnyamata ndikudziwa sungakhumbire kuzakwatira mkazi wamwana kale ndichifukwa ukundikana".........

" Ainso koma Lita iweyo sunayambe waswapo mtima wamamuna komano ineyo ndinamuswerapo mtima mkazi wina wake ndifukwa ndimaziimba mlandu monga ndimakuuzira muja nde panopa ndinangopanga chisankho chokhala kutali ndi mkazi aliyense nde sindinakonzeke tu panopa kukhala ndi chibwezi,,,, ndikuuze mene zinakhalira..... .
Ndimaphunzira School inayake ndipo inali Boarding nde kumeneko ndinapeza Chibwezi ndipo timakondana ndi mtima onse wina ndi nzake, timanvana popanda chovuta chili chonse ndipo mkati kati mwa Ulendo wathu. tsiku lina ndili ku Hostel ndinalandira message kuchokera kwa Bwenzi langa uja (Hassan mwezi wanga watha koma sindikusamba ), kunena zoona chikondi chitafikapo tinafikanso potailira kuiwala zoti tili pa school kumangozinva ngati ndi Banja basi ndipo titapita kuchipatala zinapezeka kuti Mkazi uja anali ndi Mimba, Zinali Zopatsa mantha kumene podziwa kuti Tonse ndi ana tili mmanja mwamakolo komanso Za school yathu zitha kusokonekera, komabe monga mamuna ndimamulimbitsa mtima bwezi langa uja kuti awirife tigwirane manja kuti mphepo ingakule bwanji koma isatigwetse ...... Masukulu atatsekeredwa tonse tinabwelera kunyumba ndipo tonse aliyense anawuza makolo ake zankhani imeneyi ndipo tonse konse konse zina zovuta makolo zinawavuta kuvomereza kuti chifukwa chani Okhala ana a Sukulu
{KWA MKAZI }
"Mimba imeneyi pano ife ai nde ulumikizane ndi mamunakoyo pasanathe masiku atatu akhale atabwera ndi akwawo tizapange madongosolo mutengane"
{KWATHU}
" Ife ndimakolo ako ukuziwa mapezekedwe athu ndiovutirako ndikale apa unapeza mwai Uncle ako kumakulipilira fees nde izi akazinva ukugainiza kuti ziwanvekera bwino ? Komanso kumeneko oyenera kukuperekeza kumeneko ndi Uncle akowo nde ofunikira kuwafikirabe poti ndimavuto omwe waayamba " ........
Nkhani inawapeza Uncle anga komano inali nkhani yovutirako ......
***Nthawi yomwe ija mukananena kuti School simukuifuna munakanena kuti tingokupangirani za banja zinali zophweka koma apa mwationongetsa ndalama pachabe ndili Okhumudwa Nawe Hassan nde usayembekezere kuti ndingatenge nawo gawo pa zopusa zakozo Fees sindingazalipirenso komanso zimenezo uthana nazo wekha poti apano wakulu***

{INE NDI BWENZI LANGANO }
Bwezi langa: nde ndimene zililimu zitheka masiku atatu kukhala utabwera ?
Ine: mwanjira ili yonse sizingatheke ukudziwa tili ma BOMA otalika kwambiri nde apa zonse zili pamutu panga ndekuti anthu ofuna kubwera nawowo adaliranso ine mayendedwe anga nde uwapempheko akwanu andipatse masiku ochulukirako ndizikonze zimenezi......
........
Movuta momo ndinapatsidwa week koma zinthu nde sizinali mbali yanga chili chonse chimakhala chobalalika moti week imatha koma zokonzekera zili kutali ndipo mafoni anali akuvumba kuchokera kwawo kwa Bwezi langa
# week, apa yatha nde ukuti chani ? Ife siomatilamuliratu nde week ikangothanso Osazayerekeza kubwera nso kuno # #
.....
Inali nyengo yolimba mantha anga anali pantchito yomenyana ndi nthawi koma chipambano changa nde chinali kutali kuluza kunandizungulira koma mtima wanga sunalore kuvomereza kotero ndinapanga plan yoti ndingomutumizira transport mkazi wangayo angochoka chothawa kwao tizizasungana Mopanda dongosolo momo ndipo nditaimba foni .......
Bwezi langa: sindikufuna kunva mau ako
Ine: Bwanji nso Tadikira unve kaye kuti ndikufuna ndikuuze chani Chonde
'''tu tu tu tu !!!!''' foni inadulidwa mosakhalitsa ndinaimbanso
Bwezi langa: Palibe chomwe ungayankhule choti ndinganve chifukwa ndafufuza kale zaiwe ndipo ndiwe okwatira ndichifukwa ukukanika kubwera kuno nde Kwathu osazabweranso ukamakhala usamaganizenso ngati panali kali konse pakati pathu mwana akhala wanga ekha wako upanga komko ndi akazakowo Byeee
Ine: Ta ! Ta ! Ta ! ......
(tu tu tu tu !!!)
Anadulanso Foni kachikena ndipo nditaimbanso apa nde ndinali atandi Block ndipo zimatero kwa nambala ili yonse ndingaesere kulumikizana naye ngakhale mtima wanga sumavomereza ndinayesera kuzidekhetsa ndikumupatsa nthawi kuti azitolereko mtima ukatsika tikambirane ndimuuze za Plan yanga......
Kwa Miyezi inadutsa koma namba yanga ili yo block dwabe, nditaimba panambala ina tinalumikizana koma ndinapatsidwa mau Okhumudwitsa kwambiri
"" Sorry Pachikondi chako chomwe ukuyesera kuwonetsera paine komano panopa makolo anga andipezera mamuna nde p***ano tikhala tikupanga ukwati nde ngati ungamaimbe imbebe Choncho uzandisokonezera banja Chonde Osamandiimbira ndikutumizira zithunzi za Mwana wako Umuone koma zozakumana naye nde uiwale .......
...........
Hassan: Eyetu Lita nde ukamayankhula za Mwana wako inenso ngati Bambo ndikudziwa mene umanvera mtima wa Kholo pamwana nde imeneyo si Vuto loletsa pakati paiwe ndine komano.....
Lita: komanso chani ?? Vuto siiweyo Chabe yangokhalanso nkhani yako yo yobalalitsa nde zilibwino kuti apa aliyense wanva mbali yanzake, ndikakhala ine chiganizo ndichopanga panga kale nde ndikhala ndikudikira iweyo ndinve maganizo ako ..............
Nane ndinve Maganizo anu awerengenu Eti Bwaaa Kuwerenga Ngati Ukuwonera eti 🤗😁

Nde Hes ameneyo 💥💥💥

11/06/2025

It's Tuli Day 😍
Happy BIRTHDAY To Me
🎂

10/06/2025

Ndi Mawa tu tsiku lija 😊🎂

Nde mwati tima part titatu tonseto tizaponyedwe mawalo like

Morning; Part 1
Evening; Part 2
Night. ; Part 3

Kapena zizakhale motani ndiuzeniko ndinvere maganizo anu

08/06/2025

Pamene kwangotsala 3 Days, ndiloreni Ndiulure _Story

BROKEN PARTY

🤗😁

Tandiuzeni mene mwainvelera Title ka story kake kangakhale kotani

👇👇👇
Drop your Comment

03/06/2025

Waiting for 11 June, My Tulii Day 😍
🎂

Gift Yanga Kwama Follower nonse ndakukonzerani ka Short Story mwina Kazakhala ka Ma Part atatu Okha
Tsiku lili lonse ndikhala ndikukuuzani Title yake maka ndikaiyamba Kulemba 😍😍😍

01/06/2025

Birthday ya Admin wanu nde yayandikira tu mwakonzeka kumupangira chani anthu abwino inu 😊

24/03/2025

Ambiri atangoona post kamtima kanali dyoko dyoko kuti kapena ndi Who Love Me uja waukanso 🫣 ,, mapempho Ochuluka kwambr abwera kuti nkhani zikuyenera zizibwera ndipo nditadandaula kuti Corner imodz ya page yi inagumuka ndi cyclone Hes, anthu Ali iyai ingopangitsani Fundraising pakutha week page ikhale itamangidwa ndipo nkhani zilowe m'bwalo mwaukali. So !,
Mbale yachopereka ndiimenei #0994164307

23/03/2025

Mukapeza nthawi Munvereko Nyimbo ya
"Joe Kellz ft Eli Njuchi _ Nthawi"
Mwina muikonda kuti nthawi inayake muzaigwiritse ntchto

Big shout out to my newest top fans! 💎 Mustaffa Yassin, Carolina Chilomo, Esther Banda, Maganizo Phiri, Grace Bulawayo, ...
21/03/2025

Big shout out to my newest top fans! 💎 Mustaffa Yassin, Carolina Chilomo, Esther Banda, Maganizo Phiri, Grace Bulawayo, Faith Chitani Gama, Phushe Wa John Mwasangu, Lreen Francisco, Madala Vicky, Sakina Amidu, Andrea Lekiam, Nayuma Nayu

Drop a comment to welcome them to our community, fans

Address

Area 10, Machinjiri
Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when BEST HES's stories posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Establishment

Send a message to BEST HES's stories:

Share