14/06/2025
SECOND PART OF BROKEN PARTY 🔇🔇🔇🔇🔇
Story written by HENRY MKWAILA...🖊️
CONT.
Hassan: Chabwino ndanva Maganizo ako nane ndimasaka True Love
Lita: Wow Ngati kutulo, sindikukhulupilira kuti ndakuwinadi ....... ..
Moyo wamuchikondi unayambika zonse zimayenda bwino aliyense nde amakhutira kuti akupatsidwa True Love ija moti Sitimalora kusowana kwakanthawi, nthawi zonse ma foni amakhala ali mmanja Kuyankhulana ngati tikuonana maso ndi maso kotero zoti tili motalikanabe sizimaoneka ......
....
Tsiku lina ndili khale ndinalandira Foni kuchokera kuja ndinakapanga Interview kuja yondiitana kuti ndikayambe ntchito ndipo ndinasangalala mnajowajowa anga kamwana kang'ombe, mosachedwa ndinamuuzanso Lita ndipo naye anazikonda....
Kuchokera nthawi yomwe ndinayamba ntchito zinthu zina ndi zina pakati pa ine ndi Lita zinayamba kusintha monga kuyambana yambana kunayambika ndipo kumachitika pafupi pafupi chifukwa samandinvetsetsabe kuti andipatse mpata ogwira ntchito chifukwa ndikachedwa Kuyankha foni yake amazinva ngati ndasiya kumukonda, kwa ineyo ndimazinvetsetsa komano ndinazivomereza kuti ndizikhala Kaye ngati ndaipa koma mwina akazindikira andinvetsetsanso naye komanso azolowera komabe ai ndithu pena zimazakhala ngati wayamba kundinvetsetsa koma pena umazakhalanso Moto komabe Chikondi Chathu chimapita Chitsogolo
Hassan: Wachikondi wanga ndaganiza Zoti tikhale Moyandikana mwina zitithandizira kuchepetsa mikwiyo
Lita: Zoona Wow! My Handsome ndachita kunva kukoma Pali ponse thupi langali mmh Nsane iwe ndi mdalitso mmoyo mwanga, umaziwa Kukonda ndipo wakwanitsa Kuziwa Zosowa zanga iwe ndi king wanga
Hassan: Wakondwa tu
Lita: Eya ndipo apa nde mwezi wamawa Birthday yako ndizomwe ndimakhumba ndikufuna nzapangitse Party tizasangalalire kubadwa Kwako ndipo usadere nkhawa chili chonse ndizapanga ine
Hassan: umapangiranji zonsezi zomwe ndimayenera ineyo ndizikupangira iweyo ?
Lita: ine ndinakonda mtima wako basi
......
Tinakambirana zambiri pamenepaja chinatsalira ndikumangodikira masiku kuti tikafike ku tsiku Lolonjezedwalo ndipo kwaineyo ndimati ndikalingalira ndimaona kukhala tsiku lokoma komanso lapamwamba izi zinandipangitsa Kuona Kuchedwa .....
Tili mkati modikilira ...
Weekend ina ndinaganiza zopita kumudzi kukawona makolo ndipo nditafika kumene kuja ndinacheza bwino bwino kufikira nthawi yomwe ndinafuna kubwelera komwe ndimakhala koma ndisananyamuke amai anandiimitsa mooneka kuti pali chomwe chachitika ndipo nkhani yake ndiyaikulu ndipo zokhazo zinali zokwanira kuti mtima wanga uthamangitse Mwanzi kupopa mwankhanza muja .......
Mai: Kodi nthawi ina yake unangoti ukufuna ukwatire wapeza mkazi ndizoti unali serious kapena zanthabwala
Hassan: mmh Amai nkhani ngati imene ija ndikakambe zanthabwala? Komano chachitika ndichani ?
Nditawafunsa anangondionetsa nambala ya foni kenako mkuzandifunsa kuti ndikuiziwa nambala imeneyo ndipo ndinawauza kuti Eya .....
Mai: Munthu ameneyu anaimba nde anafotokoza zoti ndi mkazi wako nde ndichifukwa ndakumbukirano kuti unayankhulapo zoti wapeza mkazi komano tisanapite patali kodi Mkazi ali ndi mwana wako uja zili pati pano
Hassan: Choyamba ndiuzeni kaye mwamuyankhula kuti chani Lita??
Mai: ndakufunsa nde ungondiyankha
Hassan: Amaiiii !!!! Oh Komano mukuziwa kale mene zinakhalira ndinamuiwala kale kale pano munthu anandiuza ekha ndikamwa yake Kuti amupezera mamuna ndipo ndisamaimbe ndimusokonezera banja mpaka pofika kundi block nde ine ndikanatani basi nane mnamuiwala apa ndapeza nzanga amene ndikunvetsetsa naye
Mai: zinatero mwina ndi eya komanso ndi Ai mwina amangoyankhulira Kupsa mtima komano zinakhalabe bwino chidzukuli changa cho chidzidzakwanitsa kuwayendera agogo akene zamaudanizi sizindisangalatsa ine
Hassan: Amai mwini chisankho ndine ndisiyeni, kodi simungasangalare mutamandiona ndili wachimwemwe ?? Mmansangalala ndikamakhala muzinkhawa ?? Tayeseraniko kusamalanso zachimwemwe ndi mwana wanune, kukazakhala kwa Mwai chidzukulu chanucho nzakachitenga muzizamuona mene mungafunire Komanso ndi Lita tizakupangirani Chizukulu
Mai: Uziyankhula mondipatsa ulemu ndine mayako
Hassan: Eya koma nanu mukuyenera kusamala zachimwemwe cha Mwana wanu Lita ndimamukonda ndipo amandikonda
Mai: nde ukupita tisanamalize kuyankhulana ? Paja nawe suchedwa Kupsa mtima koma ukanabwelera tizilongosore zimenezi .....
.......
Ndinakanika kuwayankhanso pamene paja mpaka ndinanyamuka titakwiitsana, ndinali Obalalika ndi Okwiya mutsiku li, ndipo nditangofikanso kunyumba Lita kumaimba Foni .....
Lita: tsiku lonse osandiyankhula? Komano mwangoyenera Pepa sindimaziwa kuti uli ndi Banja
Hassan: zimenezo nso nde ziti ?
Lita: Mmh Zitaye komano lero ndinayankhula ndi amai andiuza kuti uli ndi Mkazi komanso mwana
Hassan: Mau anga ndiopanda Ntchito kwa iwee kodi ?? ndizomwe umaimbira foni kuti uzindifufuza ?? Chabwino ulibe nthawi yondifunsa koma kundifufuza nde pitiriza zomwezo Osandibhowa nso apa
Lita: iiiiih Hassan ndimakukonda sinati ukwiye apa ine
Hassan: Bola wadziwa kuti ndili ndi mkazi nde mwina nthawi inakuchepera zifufuza kaye kuti ndine Otani ndikupatsa 35 Days I think panopa tipatsane kaye nthawi kuti aliyense amuziwe nzake kenako tizizawona chitsogolo kuti Chikondi chathu ndichotheka kapena ai
Lita: Eya ndiza bho bho basi tiyeni tidikire masiku wo ......
....
Chikondi chinafika Popempha Break ,,,
Moyo unali owawa pokhala mozisowa zomwe ndinazolowera kufikira pomwe ndinakanika kupilira mpaka ndinamuhalla Lita kuti ndiziwe za Moyo wake
Hassan: apa tili pa half ya 35 Days ija Nde tandiuze moyo wako ukuyenda bwanji ?
Lita: nthawi zonse umayenda bwino
Hassan: Ooh owo ndekuti zili bwino Chabwino ndimafuna ndiziwe kuti munthawi imeneyi ngati ufunikire njira zina zopezera ma information okonzera ubale wathu ....
Lita: sindikufunikiranso kali konse ndipo ndikafuna kachani ngati pakati pathu pali ubale uli onse ?
Hassan: Ukutanthauza chani
Lita: kodi mesa unathetsa Chibwezi nde sizofunikira zimenezo zipangani zoti zizikuthandizani mukafuna ine tingathe kungokhala ma friend chabe kucheza ndiza bho bho
Hassan: Aaah iweee ashiiiii bwanji ukupitiriza kuononga zinthu ? Ndimaganiza kuti kwanthawi ndinapereka ija zitithandiza kudekhetsa mitama yathu ndipo aliyense akwanitsa kuzifufunza vuto lake ndikulikonza koma ayi ndipamene zikuonongekerabe nditani kuti zikonzeke
Lita: Aaah usapange kali konse zisiye Choncho tiyeni tizingocheza basi ngati wina ndi nzake
Hassan: Oh zikomo Pachimenecho koma sizofunikira nde zitaye Basi amoyo salekana tizaona ukhale ndi nthawi yako yopambana
......
Ndinayankhula ngati zukoma koma mumtima misozi ikutsika, Moyo sumakoma nso. Masiku amapitadi ine ndi Lita kuli ziiii .... Masiku a Birthday yanga anayandikira ndi azizanga omwe ndinawaziwitsa za Party anayamba kundifunsa zamadongosolo ngakhale ndimawayankha zosanveka koma ndimawalimbitsa mtima kuti chili chonse chili Set ......
Tsiku litafika Sindinavute vute Tinapeza Dj wazoimba zabwino komanso kugula zakudya ndizakumwa kuti Chikondwelero chichitike Monga ndimkakhumbira Lita ali pambali panga tikusangalalira limodzi tsiku li koma ngati mmaloto ndimangoona chithunzi thunzi chake chokha, kotero zinandivutabe kukhala pamalo paja ndipo ndinachokapo kuwasiya anthu ali mkati mwa madyelero ndikumwelera uku choimba chikusinja zantchito zija .... Nthawi itafika yoti andifunire mafuno abwino anthu anali odabwa kuti sindimaonekapo ndipo mchimwene sanachedwe koma kuimba foni kufunsa zakomwe ndili .....
"" Oh sorry mchimwene koma sindikwanitsa kupanga nawo zimenezo ndipo ndatalikira basi kwaine ndizosakwanira kupezeka pamenepo""
Mau wa Mchimwene anakhumudwa nawo ndipo foni isaduke ndili mkati monvetsera anayankhula tu kwa anthu onse omwe anabwera ku party yi
"Party yi ithere p***a basi this is BROKEN PARTY 🔇"
END OF STORY