17/06/2026
Munthu m'modzi wamwalira ndipo ena avulala pa ngozi ya minibus yomwe yachitika ku Chiwembe, mumzinda wa Blantyre.
Malinga ndi apolisi, ngoziyi yachitika m'ma 08:00 m'mawa pa msewu wokhotera ku bwalo la zamasewero la Chiwembe.
Wachiwiri kwa Mneneri wa Polisi ya Limbe, Sub-Inspector Demetria Banda, wati minibus ya nqambala BN2417, yomwe imakachokera kwa Bvumbwe kupita ku Limbe ndipo inanyamula anthu 16, inkayendetsedwa ndi a Bosco Chazama.
Banda wati galimotoyo itafika pa mphambano yokhotera ku bwalo la Chiwembe, dalaivalayo analephera kuiongolera bwino chifukwa mabuleki sanagwire ntchito.
Zotsatira zake, minibusyo inatsetseka ndikugwera mumtsinje wa Chiwembe, zomwe zinapapangitsa kuti anthu onse omwe anali mโgalimotomo avuwlale mosiyanasiyana.
Pakadali pano, apolisi akupitiriza kufufuza chomwe chinayambitsa ngoziyi.
Bvumbwe Tv