10/05/2026
NKHANIYI NDATENGA KU PAGE YA Rodwell Lumbe
Mwana mukumuona pa pachithunziyu Anayamba kudwala ali ndi miyezi 5 chabe pamene adayamba kusintha thupi kumamela tizinthu tolimba takuda. Munkupita kwa nthawi, diso lakumanja lidatupa nkudzaphulika, ndipo kuchipatala adawauza kuti laonongekeratu mpaka adalichotsapo. Uyu ndi James (7) ndimwana m'modzi yekhayo wa Mayi Brown.
Kenako adadzatuluka nyama pamphunopa imenenso idaphulika. Adakamuchitanso operation, ndi m'mutu mwake. Panopa James sakupuma bwinobwino kudzera m'mphuno mwake monga zimayenera kukhalira. Akumabanika pafupipafupi makamaka akamagona.
Pamene zonsezi zikuchitika, ndekuti diso lake lotsalalo linayambanso kutupa kufikira pano pamene sakuoneratu mpang'ono pomwe.
Kuchipatala ndikumene akumapitaku koma sadawatsimikizire kuti akudwalayi ndi nthenda yanji kotero sizikudziwika kuti ziri ndi mankhwala izi kapena ayi. Nthawi ikupita, zambiri zikuchitika pathupi lamwanayu koma salandira thandizo lirilonse la mankhwala ayi, amangokhala.
Lachiwiri likubwerali akukalowanso ku operation ku KCH kuti akachotse diso lotsalalo ndikukonza pamphuno pake, according to the mother.
Ncholemera ichi kwa Mayi Brown. Ngati tingathe, tiyeni tinyamuzane nawo m'mene tingakwanitsire.
Tiyeni tipemphere nao limodzi, amene tidazionako izi tiyeni tiwapatseko uphungu oyenera. Ofuna kuwayendera, amakhala ku Area 44 ku Lilongwe.
Ofuna kuwafunsa zambiri, kapena kuwathandiza ndi kangachepe, phone number yawo ndi 0998 894 982.
Ngati muli ndi maganizo pankhaniyi, kapena mukufuna kuyikapo dzanja lanu mwazina, yankhulanani ndi Rodwell Lumbe pa 0995 88 00 45