19/06/2026
Akuluakulu oyang'ana za mpira m'boma la Dedza lero anali pa Kanyenda, kukhazikisa Kanyenda zoni. kumeneko mwa Zina kunali kusankha adindo monga Chairman, GS, Treasure komanso ma committee members okwana 6
Awa ndi anthu amene aziyendesa chilichonse chokhuzana ndi mpira ku zone imeneyi, izi zikuthanthauza kuti from KASUMBU to NAKAONA omwe aziyang'anila mpira ndi iwo
Mwa Zina osankhidwawa apasidwa mwayi oti azitha kufikira ma bwana omwe ali ndi chidwi chofuna kutukula ma sewelo kudera limeneli, iwo awuzidwanso kuti pachilichonse chomwe chitika akuyenela kumasamala malamulo a mpira
iwo ati akufunitsitsa kuti team yomwe izichita bwino kuzone izikhala ndi mwayi okakumana ndi ina kuchokera ku zone ina, ndipo ikapitilira izita kukamananso ndi ina mpaka kukafika kumtunda.
Kuwonjezera apo achenjeza ma team onse amene azinyanyala ndikuluka mground kuti azikhala kuti aluza or zitakhala kuti amatsogola ndi zigoli 10. mmalo mwake ati ngati team ili ndi dandawulo izipeleka madando ake kwa omwe akuyang'anira game ndipo masewelo azipitilira. zambili zili mu audio yomwe tiyituluse posachedwapa STAY TURNED