26/07/2026
AKAMALIZA KUNENA ZOIPA ZANGA BY Vindicator De poet
Akakunong'onezani izo ndidamulakwira,
Pena mwina ndidamuponda phazi,
Nthawi ya kusadziwa Yehovah polekerera.
Akakubwatikani ndi bodza la mnanu
Akafasa kundijeda ndi mijedo ya ndi
Akandisosola ndi miseche.
Dzina langali akalidesa ndi phulusa
Mawu angawa akawasokoneza pomata ndi phula,
Zomwe ndidachita akazikhotesa,
Onga mbatata ya ufa.
Zabwino ndidawachitira akazibisa,
Ndi malaya awo aakulu bwino.
Nakusegulirani khomo la m'nyozo,
Wondidesa ndi kundinyowesa ndi mvula,
Ati zawo zikhale za mchere,
Zanga zikhale za muwawani.
Akamaliza muwanong'oneze,
Asadye wa khwangwala mteza,
Akuuzeninso za mbali yawo,
Poti mulandu samva mbali imodzi,
Mungadzatengepo temberero.
Poti ulenje umasimba wako,
Apempheni akuuzeni zoipa zawo,
Atatha kunditseka ngati wothawidwa,
Ndi ndege pa Airport.
Atamaliza kundisala,
Ngati wodwala khate,
Akatha kunena zoipa zanga.